Добавить новость
smi24.net
News in English
Апрель
2024

Chakwera amuyamikira potumiza Chilima ku Tanzania

0

Katswiri pa ndale, Czar Kondowe wayamikira mtsogoleri wa dziko lino Dr. Lazarus Chakwera potumiza wachiwiri wake, Dr Saulos Chilima kukakhala nawo pa mwambo okumbukira umodzi m’dziko la Tanzania.

Poyakhula ndi wayilesi ya Timveni, a Kondowe ati izi zikuonetseratu ubale wabwino omwe ulipo pakati pa a Chakwera ndi a Chilima.

Kondowe watiso anthu akhala akuyankhula zosiyana-siyana zokhudza ubale wa anthu awiri-wa ndipo izi zithandizira kuchotsa maganizo olakwika omwe anthu amakhala nawo okhudza ubale wa atsogoleri-wa.

Komabe, Kondowe wapempha a Chakwera kuti asasiyire pompa koma apitilize kumawatuma a Chilima mu ntchito zosiyana-siyana.

Aka ndi koyamba kuchokera m’chaka cha 2022 kuwona mtsogoleri wa dziko lino akutuma a Chilima kuti akawaimire kunja kwa dziko lino.

The post Chakwera amuyamikira potumiza Chilima ku Tanzania appeared first on Malawi Voice.















Музыкальные новости






















СМИ24.net — правдивые новости, непрерывно 24/7 на русском языке с ежеминутным обновлением *